Mphunzitsi wa timu yaikulu ya dziko lino ya Flames, Patrick Mabedi, wati timu yake yagonja ndi timu ya Burundi kaamba kakuti siinakonzekere bwino.

Flames coach: Patrick ‘General’ Mabedi

Mabedi wati ngakhale panali zina zomwe osewera ake achita bwino, panalinso zofooka zambiri monga kuchinyitsa zigoli zomwe zikanatha kupeweka.

“Sivuto langa kuti sitinachite bwino, timuyi ili ndi mavuto ambiri, makonzekeredwe athu sanali bwino komanso tilibe otchinga kumbuyo chakumanzere okhazikika,” anatero Mabedi.

Iye wati akudziwa kuti anthu akudandaula za kusaitanidwa kwa osewera ena akale monga Gabadinho Mhango koma wati Gaba payekha sangaphule kanthu ngati nthawi yokonzekera ingakhale yochepa.

Timu ya Malawi ikuyembekezeka kusewera ndi timu ya Burkina Faso lachiwiri ku Mali isanakumane ndi timu ya Senegal mu mpikisano omwewu.

 

Sharing is caring!

Related Articles

Vitality Netball Nations Cup Live on DStv from February 1-9-

Vitality Netball Nations Cup Live on DStv from February 1-9

The 2025 Vitality Netball Nations Cup, featuring E...

Read More
Bob Confirmed Nomads Coach: Here’s Why he is the Right Choice-

Bob Confirmed Nomads Coach: Here’s Why he is the Right Choice

The appointment of Bob Mpinganjira as the head coa...

Read More
“Let Them Talk”: Gilbert Chirwa Claps Back at Critics Over Role Under Mponda-

“Let Them Talk”: Gilbert Chirwa Claps Back at Critics Over Role Under Mponda

Former FCB Nyasa Bullets and Flames star Gilbert C...

Read More
Castel Malawi sets mood for Wanderers and Mzuzu City Hammers Castel Cup final in Lilongwe-

Castel Malawi sets mood for Wanderers and Mzuzu City Hammers Castel Cup final in Lilongwe

Excitement is building up as Castel Malawi Limited...

Read More
Haiya reiterates his dream: “Flames will soon be qualifying consistently for AFCON.”-

Haiya reiterates his dream: “Flames will soon be qualifying consistently for AFCON.”

Football Association of Malawi (FAM) President Fle...

Read More