Mphunzitsi wa timu yaikulu ya dziko lino ya Flames, Patrick Mabedi, wati timu yake yagonja ndi timu ya Burundi kaamba kakuti siinakonzekere bwino.

Flames coach: Patrick ‘General’ Mabedi

Mabedi wati ngakhale panali zina zomwe osewera ake achita bwino, panalinso zofooka zambiri monga kuchinyitsa zigoli zomwe zikanatha kupeweka.

“Sivuto langa kuti sitinachite bwino, timuyi ili ndi mavuto ambiri, makonzekeredwe athu sanali bwino komanso tilibe otchinga kumbuyo chakumanzere okhazikika,” anatero Mabedi.

Iye wati akudziwa kuti anthu akudandaula za kusaitanidwa kwa osewera ena akale monga Gabadinho Mhango koma wati Gaba payekha sangaphule kanthu ngati nthawi yokonzekera ingakhale yochepa.

Timu ya Malawi ikuyembekezeka kusewera ndi timu ya Burkina Faso lachiwiri ku Mali isanakumane ndi timu ya Senegal mu mpikisano omwewu.

 

Sharing is caring!

Related Articles

Gabadinho Mhango’s future at Marumo Gallants hangs in the balance after accident-

Gabadinho Mhango’s future at Marumo Gallants hangs in the balance after accident

Marumo Gallants head coach Dan Malesela is set for...

Read More
She-Wolves defend Mo626 college basketball trophy with thrilling win-

She-Wolves defend Mo626 college basketball trophy with thrilling win

The Malawi Assemblies of God University’s (MAGU) w...

Read More
Gabadinho Mhango involved in road accident in South Africa-

Gabadinho Mhango involved in road accident in South Africa

Malawi’s national football team striker, Gabadinho...

Read More
All is set for Old Mutual’s 70th Anniversary Golf Tournament-

All is set for Old Mutual’s 70th Anniversary Golf Tournament

As commemorations for Old Mutual Malawi’s 70th ann...

Read More